Categories
News Radio Alinafe

AMBUYE TAMBALA APEMPHA ZIPANI ZAMUMPINGO KUFIKIRA ACHINYAMATA KU MAPARISHI AWO

Ambuye George Desmond Tambala, Arkiepiskopi wa Arkidayosizi yaKatolika ya Lilongwe, apempha zipani za ansembe komanso ma sisitele mu arkidayosiziyi kuti afikire achinyamata m’maparishi osiyanasiyana ndi cholinga choti azimvetsesa nkhani za mayitanidwe.
Ambuye Tambala ayankhula izi la Mulungu la Mayitanidwe, 21 April 2024 ku Parishi ya Mlare pa mwambo wa nsembe ya misa yomwe achinyamata mu Arkidayosiziyi amakondwelera tsikuli.
Malingana ndi Ambuye Tambala, achinyamata amasowa ansembe komanso ma sisitele kuti adziwaunikira pa nkhani ya mayitanidwe.
“Ndawapempha ansembe komanso ma sisitele mu arkidayosizi yathu, kuti tsiku la mayitanidwe lisathere pomwepa koma akuyenera kumawayendelabe achinyamatawa ku maparishi awo ndikuwaphunzitsa zosiyanasiyana zokhudza zipani zawo chifukwa achinyamatawa akumawasowa kwambiri, choncho ndawapempha kuti zisathere pomwepa ayi,” anatero ambuye Tambala.
Ambuye George Desmond Tambala, Arkiepiskopi wa Arkidayosizi yaKatolika ya Lilongwe
Ambuye Tambala atinso kudzera ku Arkidayosiziyi akhazikitsa gulu lomwe lidziliimbikitsa achinyamata m’magawo osiyanasiyana pa moyo wawo.
Gululi lili ndi anthu osiyanasiyana kuphatikizapo m’modzi wa akatswiri pankhani yoyimba a Ben Micheal komanso mphunzitsi wakale wa timu ya mpira wa miyendo ya dziko lino, a Young Chimodzi.
Ndipo mkulu owona za Mayitanidwe mu Arkidayosizi ya Lilongwe, bambo Kelvin Khodola apempha achinyamata kumvetsera mozama komanso kumalingalira za mayitanidwe awo.
Mmawu ake, wapampando wabungwe la achinyamata mu Arkidayosizi ya Lilongwe, Chisomo Nkhoma wayamikira pempho lomwe ambuye George Desmond Tambala apeleka, ponena kuti zithandiza achinyamatawa kumakhala ndi zisankho zabwino pankhani ya mayitanidwe akamakumana ndi ansembe komanso ma sisitele m’ma Parish awo.
Chisomo Nkhoma, wapampando wabungwe la achinyamata mu Arkidayosizi ya Lilongwe
Mwambo wansembe yamisa yokondwelera chaka chamayitanidwe unatsogolera ndi Ambuye mthandizi a Arkidayosizi ya Lilongwe, ambuye Vincent Mwakhwawa.
Mutu wa mayitanidwe chaka chino ndiwoti “Achinyamata pamene mukuyitanidwa kudzala mbeu za chiyembekezo ndi kumanga mtendere, pitani mukayitane aliyense kuti abwere kuphwando.”
Wolemba ndi Titus Jata Phiri
Categories
News

BUNGWE LA CAT LILIMBIKITSA ULIMI WA MAWUNGU AKULUAKULU (GIANT PUMPKINS)

Bungwe la Centre for Agricultural Transformation (CAT) lapempha alimi m’dziko muno kuyamba kubzala mbeu ya maungu akuluakulu (Giant Pumpkins) ndi cholinga chofuna kuchepetsa njala yomwe imakuta dziko lino chaka ndi chaka.

Izi zayankhulidwa lachisanu pa 16 February 2024 pamwambo wachionetsero cha mbewu ya mawunguyi, yomwe ikutchedwa NRC Giant Pumpkin, yomwe inalimidwa miyezi ingapo yapitayi ku munda wachitsanzo wabungweli ku NRC m’boma la Lilongwe.

M’modzi mwa akuluakulu a bungwe la CAT, Mayi Lizzie Kachulu ati mawunguwa athandiza alimi kukhala odzidalira pa chakudya komanso chuma.

Iwo ati kucha msanga kwa mbewuyi ndikothandiza anthu ambiri maka m’miyezi yomwe njala imavuta ya Janyuwale komanso February.

“Mawungu amenewa ndi osiyana ndi amene alimi amabzala, awawa ali ndi dzina loti Giant Pumpkins (Mawungu akuluakulu). Alimi akakhala kuti asamala bwino, ayika manyowa okwanira amalemera kuyambira ma kilogalamu atatu mpaka 30. Ndipo chimene timafuna kuti alimi adzaone ndi choti atati alimi apatsidwa mbeu iyiyi, mabanja awo atha kukapindula,” anatero a Kachulu.

Mayi Lizzie Kachulu, Mmodzi mwa akuluakulu a bungwe la CAT

 

M’mawu ake, m’modzi mwa akadaulo pankhani za ulimi ku sukulu ya ukachenjede ya NRC, Shaibu Kananji ati mbewuyi ili ndi kuthekera kothandiza alimi kupeza phindu lochuluka pa ulimi wawo.

Iwo anatsindikanso kunena kuti mbewuyi sinapangidwe kuti idzalowe mmalo mwa mbewu ya mawungu yomwe ilipo kale koma kuti ithandize alimi kukhala ndi chakudya chokwanira.

“Cholinga kwenikweni ndi chonena kuti, chifukwa choti mawungu awawa amabereka mwansanga ndi ambiri (akuluakulu komanso olemera), mlimi atha kupindula kwambiri. Mlimi atha kusankha kuti akabzale mawungu a local aja mmene amadzalira, koma awawa akabzaleso pamalo pomwe sipafuna pakhaleso chimanga ayi,” anatero a Kananji.

Shaibu Kananji, mmodzi mwa akadaulo pankhani za ulimi ku sukulu ya ukachenjede ya NRC

Poyankhulapo pambuyo pachiwonetselochi, mfumu yaikulu Mazilo 2 yayamikira mbewuyi ponena kuti iwombola anthu ochuluka omwe amakumana ndi njala chaka ndi chaka.

“Mawungu amenewa ndi osiyana ndi amene timakumana nawo makukamu (ana akwanire), awawa ndi mawungu oti nyumba anthu akaphika kaya muli anthu 10, dzungu limodzi litha kuwaombola onsewo,” anamaliza motero a mfumu Mazilo 2.

Mfumu yaikulu Mazilo 2, imodzi mwa mafumu omwe anali nawo pachionetsero cha mawungu akuluakulu

Bungwe la CAT likugwira ntchito ndi magulu osiyanasiyana pantchito yopititsa patsogolo ulimi pogwilitsa ntchito njira zamakono pofuna kuti mzika za dziko lino zisiye kudalira mtundu umodzi wa mbewu.

 

 

Wolemba: Eric Norman Mkwaira

Categories
News

CHIPANI CHA A SISTERE CHA M.M.M CHAYAMIKILIDWA KAMBA KA NTCHITO ZAKE MU ARKIDAYOSIZI YAKATOLIKA YA LILONGWE

Wolemba ndi Sam Kalimba
Arkidayosizi ya Lilongwe yayamikira ndi kulimbikitsa a sistere a chipani cha Missionaries of Mary Mediatrix (M.M.M) kamba ka utumiki wawo womwe ati akuwugwira modziyiwala mu Arkidayosiziyi.
Arkiepisikopi wa Arkidayosiziyi George Desmond Tambala ndiwo ayankhula izi pa mbuyo pa mwambo wa Misa ya malumbiro oyamba a Sr. Apronia Mahowe ndi Sr. Stella Mkwezalamba a chipanichi ku parish ya Kaggwa Loweruka pa 27 January 2024.
Ambuye Tambala anati iwo akudziwa bwino m’mene amayi achipanichi akugwirira ntchito zothandiza anthu pachipatala cha Mlare.
M’mau ake, bambo mfumu wa parish ya Andrea Kaggwa Woyera Monsignor Patrick Thawale wayamikira ntchito zomwe amayiwa akugwira pa parishiyi monga kuphunzitsa ana pa sukulu ya Wisdom Center komanso kuthandizira pa misa za ku ma outstation.
Mayi mkulu wa chipani cha Missionaries of Mary Mediatrix Sr. Mercedes Arbesu ochokera ku likulu la chipanichi ku Spain anali nawo pa mwambowu.
Categories
News

BISHOP MWAKHWAWA ENTREATS THE YOUTH TO RESPOND TO THEIR VOCATIONS

By Tiyamike Chisale

The new Catholic Bishop in Malawi, Rt. Rev. Vincent Mwakhwawa has highlighted the need for the youth to respond to their vocations in accordance with what their hearts suggest.

Bishop Mwakhwawa made the sentiments on Sunday 28th January 2023 at St. Paul Parish in Nkhotakota during his thanksgiving Mass at his home village as Auxiliary Bishop of the Catholic Archdiocese of Lilongwe.

His Lordship urged the youth to be careful when making their decisions citing that there are dangers that come after failing to respond to their calling.

The Lilongwe Archdiocese auxiliary bishop among others shared his joy for being at his home parish with family and friends to thank God for the gift of leadership which was given to him.

“This was really great day where I had to come here at my home parish in Nkhotakota to offer thanksgiving mass for the leadership in the church and the gift to the church,” said Bishop Mwakhwawa.

Rt. Rev. Vincent Fredrick Mwakhwawa was consecrated as Auxiliary Bishop of Lilongwe on 20th January 2024 at Civo Stadium in Lilongwe.

Bishop Mwakhwawa is also expected to offer another thanksgiving Mass in Karonga district, where his parents came from originally.

 

Categories
News

PRESIDENT CHAKWERA ELEVATES TA BWATALIKA TO SENIOR TA

Government has asked traditional leaders in the country to lead in uniting the citizenry in order for the country to prosper.

Minister of Local Government and Unity, honorable Richard Chimwemdo Banda made the remarks on Thursday 28th December 2023 during the elevation of Traditional Authority (TA) M’bwatalika to Senior TA M’bwatalika at Mtunthumala headquarters.

Chimwendo has also cited the need for the leaders to help in making sure that there are sustainable developments in their areas.

He said that chiefs must play a vital role when it comes to, for example, checking that the AIP program benefits the targeted groups and not vendors.

“It is the expectation of all Malawians that chiefs will allow people to live happily in all areas. They have to accommodate all people irrespective of their differences in tribes and races. They have to unite all people because we are a mixed race. They have to lead in development initiatives like buying of AIP and maize in ADMARC depots,” said Banda.

In her remarks, the Member of Parliament for the area who is also a minister of Gender and Social Welfare, honorable Jean Sendeza has urged the senior chief to work hand in hand with the government in promoting development and help in ensuring that child marriages have come to an end.

“I now advise the senior chief to be hard working, humble, accommodative and really humane. I ask her to work tirelessly for the people of her area and help other chiefs to bring the development activities needed. I also ask her vehemently to assist in ending early marriages among our girls,” said Sendeza.

Senior TA Mbwatalika whose real name is Chrisy Matiya Yelemiya has been elevated on 16th December 2023 following chiefs act chapter 22 sections 3 and 4 which give powers to the president of the republic of Malawi to elevate chiefs who among others are hardworking and of good repute.

In attendance were senior traditional authorities from Kasungu, Mchinji, Dedza and Lilongwe.

   

By Alex Nasoni

Categories
News

RBM ADDRESSES THE CITIZENRY ON A 44% DEVALUATION OF MALAWIAN KWACHA

Reserve Bank of Malawi says economic instability has for some time facilitating the trend of devaluation of the Malawi kwacha.

 

Addressing the press on Friday in Lilongwe, RBM governor, Dr Wilson Banda gave an example of the recent 44% devaluation of Malawian kwacha as a result of instability of currency at the Market.

 

Banda cited that black market has also contributed to the depreciation of the kwacha one as it cannot be controlled.

 

“The problem with these things is that you should take a position where you say you are not going to touch the exchange rate because you want to protect the vulnerable group. The position that eventually comes up is that the market does it for you. And this is when you see a black market developing and that becomes uncontrollable,” Banda said.

 

The RBM governor challenged employees not to force an adjustment of salaries from their employers as this may fuel escalation of prices.

 

He is of the view that higher wedges might force the producers to charge more on their goods in order to balance what they have invested.

 

“A wedge inflation spiral arise at a situation where workers demand higher wedges, and those higher wedges increase because of production. In order to recover the amounts that have been spent, prices have to be adjusted. That is what causes the Inflation,” he added.

 

Dr Banda among others has appealed with the public to refrain from adjusting prices of products which are made locally.

 

By Eric Norman Mkwaira